CHICHEWA RHAPSODY OF REALITIES DAILY DEVOTIONAL
Lachinayi, pa 27 November,2025
Pastor Chris Oyakhilome
SATANA ANAGONJETSEDWA KWATHUNTHU
Unali kerubi wodzozedwa wakuphimba, ndipo ndinakuika unali paphiri lopatulika la Mulungu, anayendayenda pakati pa miyala yamoto (Ezekiele 28:14)
Ngati wina angafunse kuti "nchifukwa chiyani Mulungu sanaononge satana pachiyambi?" Yankho lake limapezeka m'choonadi chimodzi chachikulu Satana anali odzozedwa. Baibulo limamutcha kuti anali "kerubi wodzozedwa..." Ndipo mbali ina ya zimene kudzoza kumachita ndi kuti kumatetezera. Mulungu anampatsa Satana mphamvu imene siyikanatheka kuyiwononga kapena kuyithetsa mwadal
Mulungu samamenyana ndi Iye yekha. Mphatso zake ndi mayitanidwe ake samasinthidwa (Aroma 11:29 CCL). N'chifukwa chake Satana sanawonongedwe. lye anali ndi kudzoza kwaumulungu kumene ngakhale kupanduka kwake sikunawuthetse nthawi yomweyo. M'malo mwake, Mulungu anayambitsa dongosolo la chiwombolo. Anamubweretsa lye amene anali wodzozedwa kuti agonjetse Satana pa Mfundo za malamulo ndi uzim
Taganizirani nkhani imene ili pa Yuda 1:9 imene imati Mikayeli mkulu wa angelo ankalimbana ndi Satana pa thupi la Mose. Baibulo limati Mikayeli sanamunene Satanayo kuti wachipongwe koma anati, "...Ambuye akudzudzule." Ndi chifukwa chakuti Satana anali atapeza udindo wovomerezeka mwa ulamuliro
Pamene Adamu anagwa chifukwa cha tchimo lalikulu lija, anapereka ulamuliro wake umene anapatsidwa ndi Mulungu kwa Satana. Satana panthawiyo, anapeza chinthu chapamwamba kuposa kukhala kerubi wodzozedwa, analandira ulamuliro wa Adamu, umene unam 'kweza ndikukhala paudindo wapamwamba kuposa angelo. Mikayeli anazindikira zimenezi. Ngakhale anali mngelo wamkulu wapamwamba, iye ankadziwa kuti zimene Satana ananena ndi zoona mwalamulo. Choncho, iye anayitanira ulamuliro wapamwamba: Dzina la Ambuye Ndipo m'Dzina limenelo, ndife apamwamba kuposa Satana ndipo timamulamulira
Choncho, chifukwa choyamba chimene Mulungu sanawononge Satana chinali chifukwa cha kudzozedwa. Chachiwiri chinali chifukwa cha ulamuliro umene Satana anapeza kudzera mu kugwa kwa Adamu. Koma dongosolo la Mulungu silinalephereke. Ambuye Yesu, Adamu wachiwiri, anabwera, wobadwa mwa Mzimu, wodzozedwa ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu, ndipo anamugonjetsa Satana mwalamulo, mwauzimu, ndi kwamuyaya. Chinthu chokongola kwambiri ndi chakuti tinachita zimenezi limodzi naye, chifukwa tinali mwa lye mu imfa yake, mu manda, mu kuuka kwake, ndi mu kupambana kwake kwakukulu pa Satana, gehena, ndi mizimu ya mdima. Choncho, INU munagonjetsa Satana kwathunthu, kotheratu ndi kwamuyay
PEMPHERO
Okondedwa Atate, zikomo chifukwa cha nzeru ndi kuzama kwa Mawu anu. Ndine ozindikira zachilungamo chanu, mphamvu yanu, ndi kudzipereka kwanu kosasinthika pa chilungamo. Zikomo chifukwa chotumiza Ambuye Yesu, Wodzozedwayo, kuti apulumutse anthu, kutipatsa ulamuliro ndi mphamvu pa Satana ndi anzake. Ndimayenda mu kupambana kumeneku lero, m'Dzina la Yesu. Amen
WERENGANINSO
Aroma 5:17; Jude 1:9; Akolose 2:15 WNT: Marko 16:
NDONDOMEKO YOWERENGA BAIBULO CHAKA CHIMODZI
2 Petro 1 & Ezekiele 37-
NDONDOMEKO YOWERENGA BAIBULO ZAKA ZIWIR
Yohane 15:11-19 & 1 Mbiri 2I*38I*17:*.*O*a.a.o.u.a._.U*e_
Yohane 15:11-19 & 1 Mbiri 27