Offline
https://public-rf-upload.minhawebradio.net/250607/slider/5925e3a30547c4e2e3d648bc4a5ed5d5.png
READ RHAPSODY Today's Devotional in Chichewa
By Blessed Tryness
Published on 12/05/2025 08:58 • Updated 27/11/2025 12:23
Rhapsody of Realities

CHICHEWA RHAPSODY OF REALITIES DAILY DEVOTIONAL

 

Lachinayi, pa  27 November,2025

 

Pastor Chris Oyakhilome

 

SATANA ANAGONJETSEDWA KWATHUNTHU

 

Unali kerubi wodzozedwa wakuphimba, ndipo ndinakuika unali paphiri lopatulika la Mulungu, anayendayenda pakati pa miyala yamoto (Ezekiele 28:14)

 

Ngati wina angafunse kuti "nchifukwa chiyani Mulungu sanaononge satana pachiyambi?" Yankho lake limapezeka m'choonadi chimodzi chachikulu Satana anali odzozedwa. Baibulo limamutcha kuti anali "kerubi wodzozedwa..." Ndipo mbali ina ya zimene kudzoza kumachita ndi kuti kumatetezera. Mulungu anampatsa Satana mphamvu imene siyikanatheka kuyiwononga kapena kuyithetsa mwadal

 

Mulungu samamenyana ndi Iye yekha. Mphatso zake ndi mayitanidwe ake samasinthidwa (Aroma 11:29 CCL). N'chifukwa chake Satana sanawonongedwe. lye anali ndi kudzoza kwaumulungu kumene ngakhale kupanduka kwake sikunawuthetse nthawi yomweyo. M'malo mwake, Mulungu anayambitsa dongosolo la chiwombolo. Anamubweretsa lye amene anali wodzozedwa kuti agonjetse Satana pa Mfundo za malamulo ndi uzim

 

Taganizirani nkhani imene ili pa Yuda 1:9 imene imati Mikayeli mkulu wa angelo ankalimbana ndi Satana pa thupi la Mose. Baibulo limati Mikayeli sanamunene Satanayo kuti wachipongwe koma anati, "...Ambuye akudzudzule." Ndi chifukwa chakuti Satana anali atapeza udindo wovomerezeka mwa ulamuliro

 

Pamene Adamu anagwa chifukwa cha tchimo lalikulu lija, anapereka ulamuliro wake umene anapatsidwa ndi Mulungu kwa Satana. Satana panthawiyo, anapeza chinthu chapamwamba kuposa kukhala kerubi wodzozedwa, analandira ulamuliro wa Adamu, umene unam 'kweza ndikukhala paudindo wapamwamba kuposa angelo. Mikayeli anazindikira zimenezi. Ngakhale anali mngelo wamkulu wapamwamba, iye ankadziwa kuti zimene Satana ananena ndi zoona mwalamulo. Choncho, iye anayitanira ulamuliro wapamwamba: Dzina la Ambuye Ndipo m'Dzina limenelo, ndife apamwamba kuposa Satana ndipo timamulamulira

 

Choncho, chifukwa choyamba chimene Mulungu sanawononge Satana chinali chifukwa cha kudzozedwa. Chachiwiri chinali chifukwa cha ulamuliro umene Satana anapeza kudzera mu kugwa kwa Adamu. Koma dongosolo la Mulungu silinalephereke. Ambuye Yesu, Adamu wachiwiri, anabwera, wobadwa mwa Mzimu, wodzozedwa ndi Mzimu Woyera ndi mphamvu, ndipo anamugonjetsa Satana mwalamulo, mwauzimu, ndi kwamuyaya. Chinthu chokongola kwambiri ndi chakuti tinachita zimenezi limodzi naye, chifukwa tinali mwa lye mu imfa yake, mu manda, mu kuuka kwake, ndi mu kupambana kwake kwakukulu pa Satana, gehena, ndi mizimu ya mdima. Choncho, INU munagonjetsa Satana kwathunthu, kotheratu ndi kwamuyay

 

PEMPHERO

 

Okondedwa Atate, zikomo chifukwa cha nzeru ndi kuzama kwa Mawu anu. Ndine ozindikira zachilungamo chanu, mphamvu yanu, ndi kudzipereka kwanu kosasinthika pa chilungamo. Zikomo chifukwa chotumiza Ambuye Yesu, Wodzozedwayo, kuti apulumutse anthu, kutipatsa ulamuliro ndi mphamvu pa Satana ndi anzake. Ndimayenda mu kupambana kumeneku lero, m'Dzina la Yesu. Amen

 

WERENGANINSO

 

Aroma 5:17; Jude 1:9; Akolose 2:15 WNT: Marko 16:

 

NDONDOMEKO YOWERENGA BAIBULO CHAKA CHIMODZI

 

2 Petro 1 & Ezekiele 37-

 

NDONDOMEKO YOWERENGA BAIBULO ZAKA ZIWIR

 

Yohane 15:11-19 & 1 Mbiri 2I*38I*17:*.*O*a.a.o.u.a._.U*e_ 

 

Yohane 15:11-19 & 1 Mbiri 27

Comments